Skip to main content

AKAPUSA MUDYERE

Misonzi yachimwemwe idatsikira mmasaya mwa Sitelia kuchoka mmaso mwake. Sadathe kukhulupirira kuti loto lake lakwaniritsidwa. Zinali ngati kuti ali mtulo ndipo ali kulota. Chapatali potero Waisoni adakhala chete mkumaonerera mwambo wonse wa ukwati wa mkazi wake wa kale. Adakumbukira mmene amkamutukwanira komanso kumunyoza mkazi yo pa nthawi imene adali limodzi, mtima wake udagunda koposa ndipo anamva kuwawidwa. Kwa iye mkazi anali kalopo koposa ndipo amkakhulupirira kuti kumtchenetsa mkazi Kapena kumuyambitsa bizinesi kunali kutaya nthawi komanso kuononga ndalama chabe. Tsiku liri lonse Sitelia adali akukhala odandaula ndinso kugona ndi njala limodzi ndi ana ake awiri pamene Waisoni adali kupita kuzisangalalo kumene amakadyako mang'ina, zibwente, tchipisi ndi fuloze. Amkapita kunyumba atakhuta ndipo amkangofikira phiii kugona. Khalidwe li mkazi atafika potopa nalo anayamba kuyenda yenda mnamakasaka chakudya cha iye ndi ana ake ndipo waisoni analibe nazo ntchito. Pamene mkazi yu adakali pakati posaka chakudya adakumana ndi chikhwaya chogwira ntchito mu banki, adakondana ndipo ubwenzi udayamba. Kwa miyezi ingapo ubwenzi wawo udakulira ndinso kutentherera koma zonsezi Waisoni sadali kuziwa pakuti samkakhala pakhomo tsiku lonse. Usiku wina mwachidzolowedzi adangodabwa kufika pakhomo mkupedza kuti mkazi wake komanso ana palibe. Adayang'ana muzipinda zonse za mnyumba mo ndipo sadawapedze, adakhala pabalaza mnawadikirira koma mawola awiri adadutsa ndipo iwo sadatulukire, adaganiza zopita kuchipinda kumene iye ndi mkazi wake Sitelia amkagona ndipo adali ozizidwa nkhongono kupedza chibaluwa chomwe mkazi yo adalemba kumusanzika kuti wapita kukaona patsidya la nyanja pamodzi ndi khadi lomuitana ku ukwati omwe mkazi wakeyo adali kuchita lachiweru lomwe lidali kudza. Izi zinamuvuta Waisoni kukhulupirira ndipo lisipa ndi mutu wa ching'alang'ala zidamupedza.  Adakanika kumvetsa kuti mkazi wakeyo wapitadi ndipo adawona kuchedwa kuti lachiweru lifike akazionere yekha ngati zinalidi zoona. Tulo tidamusowa. Adakhala akulingalira komanso Kulira kuti zibwana zake zamuthawitsira mkazi ndi ana omwe. Tsiku lo litafika Wasioni adakonzeka molawira koposa ngati mwina ukwati wo udali wake ndipo adalunjika Ku kachisi imene ukwati wo umkadalitsidwira. Mmimba mudaotcha ndipo adaona ngati chifunga komanso anamva kutentha mthupi mwake monse pamene adawona mkazi wake Sitelia ali mu Velo loyera bwino ngati ngelo, maphodedwe amene adali pa thupi la mkazi yu adamupangitsa Waisoni kubwera mkhwidzi yomwe adakanika kuitula pakuti kupusa kwake mkomwe kudapangitsa kuti ena amulande mkazi.  Adalaka laka atatsatira mkazi wake yo kutsogolo pamene m'busa adafunsa ngati analipo wina oletsa kuti awiri wo asakhale limodzi ngati banja. Koma kunali komuvuta zedi Waisoni kutero pakuti miyendo yake komanso minyewa yonse idali itafooka koposa ndipo mphamvu zoimirira adalibe pakuti adali kuopa kuti atha kuchitira chimbuzi mukachisi mo kaamba ka mantha komanso mkwiyo ndi manyazi omwe adali nawo. Apa mpamene Waisoni adadzindikira kuti munthu di akapusa amadyeredwa ndithu ingakhale mkazi amene.. CHENJERA!!!!


THE END!

Comments

  1. Wow!!! You have put a lot of work into this piece and phunziro lalikulu heavy. Keep up the good work 💪💪💪

    ReplyDelete

Post a Comment

Popular posts from this blog

AWAKENING: STORIES UNTOLD, STORIES UNHEARD AND STORIES UNREAD

Correct me if I am wrong, but I remember all the words you like to say behind closed doors. She whispered in my ear “I take you as you are and you will be. I won’t try to change you but I will ride out change with you. I see you and I will never ask you to be less or more.” With words so charming and full of meaning, that’s how she destroyed me. I have been awed and terrified by the experience of being in love to the extent that when it’s love, I’d rather close the book and put it back on the shelf. I do not know how to hate no matter how much I have been wronged. I met Tuseke when I had gone for my usual check-up at the hospital. She was there to visit her grandmother who was gravely ill and on admission. She had asked for directions to get to the elderly female ward, that was just the same way to Doctor Mayepi’s office. My all time go to health practitioner. We walked hand in hand and talked about a few things on science and medicine. She hated being around the hosp...

LOVE LETTER TO TOBI

  Tobi; You are the chapter that I didn’t know it’s words. No matter what takes place, my heart will always choose you. Like a bedtime story book, I will open my chest and read to you all my love. I said; “I want to relearn love in a beautiful way.” and I knew the universe remembered me the day that I met you. You have given oxygen to the parts of me that were suffocated, energy to my broken bones. Your name belongs at the tip of my tongue, I want to speak of you and with you all day long cause there’s a certain kind of magic in your name. I want to wrap my entire body around yours. I want the love that ravishes and envelops me. My hands long to hold you, to lace my fingers all over your lips, to feel the whole of you on my skin, to breath your scent and fill my lungs with your precious cologne.   Kegi….

LETTER TO KAMBANI

  Dearest Kambani, I write this note to you for there is an ache in my ribs. Your sugar-coated deceit made its way through and I felt like all the air left my lungs after I heard and read out all your lies. You said; “I will answer you before you even call to me.” Little did I know you were trying to memorize Jeremiah 33:3 on me. You said; “I will be your peace.” But; Don’t be my peace. I already have that. First, be at peace with yourself and everything around you. I know this note will make you remember the warmth of my touch, how it made your heart race, the joy you claimed I brought to you. I had mixed portions of happiness and loyalty between the things I love and you with a pinch of sugar to align the moments. That’s how much I cared. I am blooming in your absence after being trapped in the cage of your lies and deceit, after you sliced me a dose of pain and moments of tears. Leaving you came hand in hand with finding myself – Broken but Function...

I LIVE

  The phase I was in weeks ago made me question my existence on earth “perhaps, has my time elapsed?” I have escaped a number of accidents for two weeks in a roll. I was on bed rest. Got back on feet and faced yet another accident day after day “I thought my life has come to an end.” “I could barely let food pass my throat; the fear-anxiety and the stress all over it of what becomes of me the next day was too much for my mind” “is death beckoning me?” I asked myself a couple of random questions just to be sure I was on a right spot - safe and sane “I must repent.” “Change my ways, stay sane even in the midst of the rumbling thunder that was ready to take over in my brain.” So I rose up, charged myself up “enough is enough.” My mother had already said a prayer of favor  over me. She blessed me right from the day I was conceived. “You shall not die before your time, you shall live to fulfill  your purpose on earth; No man anywhere will deny you of your dues, the harvest of ...

CHAPTER 28

The truth failed to set me free. I do not know how to speak the truth without it sounding like an apology, But I am learning to share the room with peace. You said these broken pieces won't fit together, But I have out grown those words and will shrink to fit, For courage has greeted me. Drop me here and leave me be, This is just a chapter not my whole story....